Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Marko 7:15-29 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

15. kulibe kanthu kunja kwa munthu kakulowa mwa iye, kangathe kumdetsa: koma zinthu zakuturuka mwa munthu, ndizo zakumdetsa munthu.[

16. ]

17. Ndipo m'mene Iye adalowa m'nyumba kusiyana ndi khamulo, ophunzira ace anamfunsa Iye faruzolo.

18. Ndipo ananena nao, Mutero inunso opanda nzeru kodi? Kodi simuzindikira kuti kanthu kali konse kocokera kunja kakulowa mwa munthu, sikangathe kumdetsa iye;

19. cifukwa sikalowa mumtima mwace, koma m'mimba mwace, ndipo katurukira kuthengo? Ndipo potero anayeretsa zakudya zonse.

20. Ndipo anati, Coturuka mwa munthu ndico cidetsa munthu.

21. Pakuti m'kati mwace mwa mitima ya anthu, muturuka maganizo oipa, zaciwerewere,

22. zakuba, zakupha, zacigololo, masiriro, zoipa, cinyengo, cinyanso, diso loipa, mwano, kudzikuza, kupusa:

23. zoipa izi zonse zituruka m'kati, nizidetsa munthu.

24. Ndipo Iye anauka nacoka kumeneko, nanka ku maiko a ku Turo ndi Sidoni, Ndipo analowa m'nyumba, nafuna kuti asadziwe anthu; ndipo sanakhoza kubisika.

25. Koma pomwepo mkazi, kabuthu kace kanali ndi mzimu wonyansa, pamene anamva za Iye, anadza, nagwa pa mapazi ace.

26. Koma mkaziyo anali Mhelene, mtundu wace MsuroFonika. Ndipo anampempha Iye kuti aturutse ciwanda m'mwana wace.

27. Ndipo ananena naye, Baleka, athange akhuta ana; pakuti si kwabwino kuti titenge mkate wa ana ndi kuutayira tiagaru,

28. Koma iye anabvomera nanena ndi Iye, inde Ambuye; tingakhale tiagaru ta pansi pa gome tikudyako nyenyeswa za ana.

29. Ndipo anati kwa iye, Cifukwa ca mau amene, muka; ciwanda caturuka m'mwana wako wamkazi.

Werengani mutu wathunthu Marko 7