Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Marko 6:41-44 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

41. Ndipo Iye anatenga mikate isanuyo ndi nsomba ziwirizo nayang'anakumwamba, nadalitsa, nagawa mikate; napatsa kwa ophunzira kuti apereke kwa iwo; ndi nsomba ziwiri anagawira onsewo.

42. Ndipo anadya iwo onse, nakhuta.

43. Ndipo anatola makombo mitanga khumi ndi iwiri, ndiponso za nsomba.

44. Ndipo amene anadya mikate iyo anali amuna zikwi zisanu.

Werengani mutu wathunthu Marko 6