Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Marko 6:38-41 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

38. Ndipo Iye ananena nao, kuti, Muli nayo mikate ingati? pitani, mukaone. Ndipo m'mene anadziwa ananena, lsanu, ndi nsomba ziwiri.

39. Ndipo anawalamulira kuti akhalitse pansi onse magulu magulu pamsipu.

40. Ndipo anakhala pansi mabungwe mabungwe a makumi khumi, ndi a makumi asanu.

41. Ndipo Iye anatenga mikate isanuyo ndi nsomba ziwirizo nayang'anakumwamba, nadalitsa, nagawa mikate; napatsa kwa ophunzira kuti apereke kwa iwo; ndi nsomba ziwiri anagawira onsewo.

Werengani mutu wathunthu Marko 6