Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Marko 6:36-46 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

36. muwauze kuti amuke, alowe kumiraga ndi ku midzi yozungulira, akadzigulire okha kanthu kakudya.

37. Koma Iye anayankha nati kwa iwo, Apatseni kudya ndinu. Ndipo iwo ananena naye, Kodi tikapita ife ndi kugula mikate ya pa marupiya atheka mazana awiri, ndi kuwapatsa kudya?

38. Ndipo Iye ananena nao, kuti, Muli nayo mikate ingati? pitani, mukaone. Ndipo m'mene anadziwa ananena, lsanu, ndi nsomba ziwiri.

39. Ndipo anawalamulira kuti akhalitse pansi onse magulu magulu pamsipu.

40. Ndipo anakhala pansi mabungwe mabungwe a makumi khumi, ndi a makumi asanu.

41. Ndipo Iye anatenga mikate isanuyo ndi nsomba ziwirizo nayang'anakumwamba, nadalitsa, nagawa mikate; napatsa kwa ophunzira kuti apereke kwa iwo; ndi nsomba ziwiri anagawira onsewo.

42. Ndipo anadya iwo onse, nakhuta.

43. Ndipo anatola makombo mitanga khumi ndi iwiri, ndiponso za nsomba.

44. Ndipo amene anadya mikate iyo anali amuna zikwi zisanu.

45. Ndipo pomwepo Iye anakangamiza ophunzira ace alowe rri'ngalawa, ndi kumtsogolera kutsidya lija ku Betsaida, m'mene Iye yekha alimkuuza khamulo kuti amuke.

46. Ndipo atalawirana nao, anacoka Iye, nalowa m'phiri kukapemphera,

Werengani mutu wathunthu Marko 6