Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Marko 6:24-30 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

24. Ndipo anaturuka, nati kwa amace, Ndidzapempha ciani? Ndipo iyel anati, Mutu wace wa Yohane Mbatizi.

25. Ndipo pomwepo analowa m'mangu m'mangu kwa mfumu, napempha kuti, Ndifuna kuti mundipatse tsopano apa, mutu wace wa Yohane Mbatizi mumbizi.

26. Ndipo mfumu inamva cisoni cacikuru; koma cifukwa ca malumbiro ace, ndi ca iwo akukhala pacakudya, sanafuna kumkaniza.

27. Ndipo pomwepo mfumu inatuma mnyamata, namlamulira akatenge mutu wace; ndipo iye anamuka namdula mutu m'nyumba yandende;

28. natengera mutu wace mumbizi, naupereka kwa buthulo; ndipo buthu linaupereka kwa amace.

29. Ndipo m'mene ophunzira ace anamva, anadza nanyamula mtembo wace nauika m'manda.

30. Ndipo atumwi anasonkhana kwa Yesu; namuuza ziri zonse adazicita, ndi zonse adaziphunzitsa,

Werengani mutu wathunthu Marko 6