Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Marko 5:9-22 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

9. Ndipo anamfunsa, Dzina lako ndani? Ndipo ananena kwa Iye, Dzina langa ndine Legio; cifukwa tiri ambiri.

10. Ndipo anampempha Iye kwambiri kuti asaiturutsire kunja kwace kwa dziko.

11. Ndipo panali pamenepo gulu lalikuru la nkhumba zirinkudya kuphiri.

12. Ndipo inampempha Iye, kuti, Titumizeni ife mu nkhumbazo, kuti tilowe mu izo.

13. Ndipo anailolao Ndipo mizimu yonyansa inaturuka, nilowa mu nkhumba; ndipo gulu linatsika liwiro potsetsereka ndi kulowa m'nyanja, ndizo ngati zikwi ziwiri; ndipo zinatsamwa m'nyanja.

14. Ndipo akuziweta anathawa, nauza m'mudzi, ndi kwninda. Ndipo anadza kudzaona cocitikaco.

15. Ndipo anadza kwa Yesu, napenya wogwidwa ziwandayo alikukhala pansi, wobvala ndi wa nzeru zace zabwino, ndiye amene anali ndi legio; ndipo anaopa iwo.

16. Ndipo adapenyawo adawafotokozera umo anacitira ndi wogwidwa ziwandayo, ndi za nkhumbazo.

17. Ndipo anayamba kumpempha Iye kuti acoke m'malire ao,

18. Ndipo m'mene Iye analikulowa mungalawa, anampempha waziwanda uja kuti akhale ndi Iye.

19. Ndipo sanamlola, koma ananena naye, Muka kwanu kwa abale ako, nuwauze zinthu zazikuru anakucitira Ambuye, ndi kuti anakucitira cifundo.

20. Ndipo anamuka nayamba kulalikira ku Dekapoli zinthu zazikuru Yesu adamcitira iye; ndipo anthu onse anazizwa.

21. Ndipo pamene Yesu anaolokanso mungalawa tsidya lina, khamu lalikuru linasonkhana kwa Iye; ndipo Iye anali pambali pa nyanja.

22. Ndipo anadzako mmodzi wa akuru a sunagoge, dzina lace Yairo; ndipo pakuona Iye, anagwada pa mapazi ace, nampempha kwambiri,

Werengani mutu wathunthu Marko 5