Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Marko 5:7-17 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

7. ndipo anapfuula ndi mau olimba, nanena, Ndiri ndi ciani ine ndi Inu, Yesu Mwana wa Mulungu Wamkurukuru? Ndikulumbirirani pa Mulungu, msandizunze.

8. Pakuti ananena kwa iye, Turuka iwe, mzimu wonyansa, kwa munthuyu.

9. Ndipo anamfunsa, Dzina lako ndani? Ndipo ananena kwa Iye, Dzina langa ndine Legio; cifukwa tiri ambiri.

10. Ndipo anampempha Iye kwambiri kuti asaiturutsire kunja kwace kwa dziko.

11. Ndipo panali pamenepo gulu lalikuru la nkhumba zirinkudya kuphiri.

12. Ndipo inampempha Iye, kuti, Titumizeni ife mu nkhumbazo, kuti tilowe mu izo.

13. Ndipo anailolao Ndipo mizimu yonyansa inaturuka, nilowa mu nkhumba; ndipo gulu linatsika liwiro potsetsereka ndi kulowa m'nyanja, ndizo ngati zikwi ziwiri; ndipo zinatsamwa m'nyanja.

14. Ndipo akuziweta anathawa, nauza m'mudzi, ndi kwninda. Ndipo anadza kudzaona cocitikaco.

15. Ndipo anadza kwa Yesu, napenya wogwidwa ziwandayo alikukhala pansi, wobvala ndi wa nzeru zace zabwino, ndiye amene anali ndi legio; ndipo anaopa iwo.

16. Ndipo adapenyawo adawafotokozera umo anacitira ndi wogwidwa ziwandayo, ndi za nkhumbazo.

17. Ndipo anayamba kumpempha Iye kuti acoke m'malire ao,

Werengani mutu wathunthu Marko 5