Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Marko 5:34-43 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

34. Ndipo anati kwa iye, Mwana wamkaziwe, cikhulupiriro, cako cakupulumutsa; muka mumtendere, nukhale wocira cibvutiko cako.

35. M'mene iye ali cilankhulire, anafika a ku nyumba ya mkuru wa sunagoge, nanena, kuti, Mwana wako wafa; ubvutiranjinso Mphunzitsi?

36. Koma Yesu wosasamala mau olankhulidwawo, ananena kwa mkuru wa sunagoge, Usaope, khulupirira kokha.

37. Ndipo sanalola munthu yense kutsagana naye, koma Petro, ndi Yakobo, ndi Yohane mbale wace wa Yakobo.

38. Ndipo anafika ku nyumba kwace kwa mkuru wa sunagoge; ndipo anaona cipiringu, ndi ocita maliro, ndi akukuwa ambiri

39. Ndipo m'mene atalowa, ananena nao, Mubuma ndi kulira bwanji? Mwana sanafa, koma ali m'tulo.

40. Ndipo anamseka Iye pwepwete, Koma Iye anawaturutsa onse, natenga atate wa mwana, ndi amace, ndi ajawo anali naye, nalowa m'mene munali mwanayo.

41. Ndipo anagwira dzanja lace la mwana, nanena kwa iye, Talita koumi; ndiko kunena posandulika, Buthu, ndinena ndi iwe, Uka.

42. Ndipo pomwepo buthulo linauka, niliyenda; pakuti linali la zaka khumi ndi ziwiri. Ndipo anadabwa pomwepo ndi kudabwa kwakukuru.

43. Ndipo anawalamulira kwambiri kuti asadziwe ici munthu mmodzi, nawauza kuti ampatse iye kudya.

Werengani mutu wathunthu Marko 5