Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Marko 5:20-27 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

20. Ndipo anamuka nayamba kulalikira ku Dekapoli zinthu zazikuru Yesu adamcitira iye; ndipo anthu onse anazizwa.

21. Ndipo pamene Yesu anaolokanso mungalawa tsidya lina, khamu lalikuru linasonkhana kwa Iye; ndipo Iye anali pambali pa nyanja.

22. Ndipo anadzako mmodzi wa akuru a sunagoge, dzina lace Yairo; ndipo pakuona Iye, anagwada pa mapazi ace, nampempha kwambiri,

23. nanena, kuti, Kamwana kanga kabuthu kalimkutsirizika; ndikupemphani Inu mufikeko, muike manja anu pa iko, kuti kapulwnuke, ndi kukhala ndi moyo.

24. Ndipo ananka naye pamodzi; ndipo khamu lalikuru linamtsata Iye, ndi kumkanikiza Iye.

25. Ndipo munthu wamkazi amene anali ndi nthenda yacidwalire zaka khwni ndi ziwiri,

26. ndipo anamva zowawa zambiri ndi asing'anga ambiri, nalipira zonse anali nazo osacira pang'ono ponse, koma makamaka nthenda yace idakula,

27. m'mene iye anamva mbiri yace ya Yesu, anadza m'khamu kumbuyo kwace, nakhudza cobvala cace.

Werengani mutu wathunthu Marko 5