Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Marko 5:1-7 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ndipo anafika tsidya lina la nyanja, ku dziko la Agerasa,

2. Ndipo pameneadaturuka mungalawa, pomwepo anakomana naye munthu woturuka kumanda wa mzimu wonyansa,

3. amene anayesa nyumba yace kumanda; ndipo palibe munthu anakhoza kummanganso, inde ngakhale ndi unyolo;

4. pakuti adafomangidwa kawiri kawiri ndi matangadza ndimaunyolo, ndipo anamwetula maunyolo, naduladula matangadza; ndipo palibe munthu anali ndi mphamvu yakumfuya.

5. Ndipo masiku onse, usiku ndi usana, anakhala m'manda ndi m'mapiri, napfuula, nadzitematema ndi miyala.

6. Ndipo pakuona Yesu kutali, anathamanga, namgwadira Iye;

7. ndipo anapfuula ndi mau olimba, nanena, Ndiri ndi ciani ine ndi Inu, Yesu Mwana wa Mulungu Wamkurukuru? Ndikulumbirirani pa Mulungu, msandizunze.

Werengani mutu wathunthu Marko 5