Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Marko 4:4-15 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

4. ndipo kunali, m'kufesa kwace, zina zinagwa m'mbali mwanjira, ndi mbalamezinadza ndi kuzitha kudya,

5. Ndipo zina zinagwa pa nthaka yathanthwe, pamene panalibe nthaka yambiri; ndipo pomwepo zinamera, cifukwa zinalibe nthaka yakuya;

6. ndipo litakwera dzuwa zinapserera; ndipo popeza zinalibe mizu zinakhwinyata.

7. Ndipo zina zinagwa paminga, ndipominga inakula, nizitsamwitsa, ndipo sizinabala zipatso.

8. Ndipo zina zinagwa m'nthaka yabwino, ndipo zinapatsa zipatso, ndi kukula ndi kucuruka; ndipo zinabala kupindula makumi atatu, ndi makumi asanundi limodzi, ndi makumi khumi.

9. Ndipo ananena, Amene ali nao makutu akumva amve.

10. Ndipo pamene anakhala pa yekha, iwo amene anali pafupi ndi Iye pamodzi ndi khumi ndi awiriwo anamfunsa za mafanizo.

11. Ndipo Iye ananena nao, Kwa inu kwapatsidwa cinsinsi ca Ufumu wa Mulungu; koma kwa iwo ali kunja zonse zicitidwa m'mafanizo;

12. kuti kupenya apenye, koma asazindikire; ndipo kumva amve, koma asadziwitse; kuti pena angatembenuke, ndi kukhululukidwa.

13. Ndipo ananena nao, Simudziwa kodi fanizo ili? mukazindikira bwanji mafanizo onse?

14. Wofesa afesa mau.

15. Ndipo iwo ndiwo a m'mbali mwa njira mofesedwamo mau; ndipo pamene anamva, pomwepo akudza Satana nacotsa mau ofesedwa mwa iwo.

Werengani mutu wathunthu Marko 4