Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Marko 4:1-4 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ndipo anayambanso kuphunzitsa pambali pa nyanja, Ndipo anasonkhana kwa Iye khamu lalikurukuru, kotero kuti analowa Iye mungalawa, nakhala m'nyanja; ndipo khamu lonse linakhala pamtunda m'mbali mwa nyanja.

2. Ndipo anawaphunzitsa zinthu zambiri m'mafanizo, nanena nao m'ciphunzitso cace,

3. Mverani: taonani, wofesa anaturuka kukafesa;

4. ndipo kunali, m'kufesa kwace, zina zinagwa m'mbali mwanjira, ndi mbalamezinadza ndi kuzitha kudya,

Werengani mutu wathunthu Marko 4