Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Marko 3:29-33 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

29. koma ali yense adzacitira Mzimu Woyera mwano alibe kukhululukidwa nthawi yonse, koma anaparamuladi cimo losatha;

30. pakuti adanena, Ali ndi mzimu wonyansa.

31. Ndipo anadza amace ndi abale ace; naima kunja, namtumira uthenga kumuitana.

32. Ndipo anthu ambiri anakhala pansi pomzinga; nanena kwa Iye, Onani, amanu ndi abale anu ali kunja akufunani Inu.

33. Ndipo anawayankha nanena, Amai wanga ndi abale anga ndani?

Werengani mutu wathunthu Marko 3