29. koma ali yense adzacitira Mzimu Woyera mwano alibe kukhululukidwa nthawi yonse, koma anaparamuladi cimo losatha;
30. pakuti adanena, Ali ndi mzimu wonyansa.
31. Ndipo anadza amace ndi abale ace; naima kunja, namtumira uthenga kumuitana.
32. Ndipo anthu ambiri anakhala pansi pomzinga; nanena kwa Iye, Onani, amanu ndi abale anu ali kunja akufunani Inu.
33. Ndipo anawayankha nanena, Amai wanga ndi abale anga ndani?