Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Marko 3:21-34 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

21. Ndipo pamene abale ace anamva, anadza kudzamgwira Iye; pakuti anati adayaruka.

22. Ndipo alembi amene adatsika ku Yerusalemu ananena kuti, Ali naye Beelzibule, ndipo, Ndi mkuru wao wa ziwanda aturutsa ziwanda.

23. Ndipo m'mene adawaitana iwo, ananena nao m'mafanizo, Satana angathe bwanji kuturutsa Satana?

24. Ndipo ufumu ukagawanika pa uwu wokha, sukhoza kukhazikika.

25. Ndipo nyumba ikagawanika pa iyo yokha, siikhoza kukhazikika nyumbayo,

26. Ndipo Satana akadziukira mwini yekha, nagawanika, sakhoza kukhazikika, koma atsirizika.

27. Komatu palibe munthu akhoza kulowa m'nvumba ya mwini mphamvu, ndi kufunkha akatundu ace, koma athange wamanga mwini mphamvuyo; ndipo pamenepo adzafunkha za m'nyumba mwace.

28. Indetu, ndinena ndi inu, Adzakhululukidwa macimo onse a ana a anthu, ndi zamwano ziri zonse adzacita mwano nazo;

29. koma ali yense adzacitira Mzimu Woyera mwano alibe kukhululukidwa nthawi yonse, koma anaparamuladi cimo losatha;

30. pakuti adanena, Ali ndi mzimu wonyansa.

31. Ndipo anadza amace ndi abale ace; naima kunja, namtumira uthenga kumuitana.

32. Ndipo anthu ambiri anakhala pansi pomzinga; nanena kwa Iye, Onani, amanu ndi abale anu ali kunja akufunani Inu.

33. Ndipo anawayankha nanena, Amai wanga ndi abale anga ndani?

34. Ndipo anawaunguza-unguza iwo akumzingawo, nanena, Taonani, amai wanga ndi abale anga.

Werengani mutu wathunthu Marko 3