Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Marko 3:15-29 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

15. ndi kuti akhale nao ulamuliro wakuturutsa ziwanda.

16. Ndipo Simoni anamucha Petro;

17. ndi Yakobo mwana wa Zebedayo, ndi Yohane mbale wace wa Yakobo, iwo anawacha Boanerge, ndiko kuti, Ana a bingu;

18. ndi Andreya, ndi Filipo, ndi Bartolomeyo, ndi Mateyu, ndi Tomasi, ndi Yakobo mwana wa Alifeyo, ndi Tadeyo, ndi Simoni Mkanani,

19. ndi Yudase Isikariote, ndiye amene anampereka Iye.Ndipo analowa m'nyumba.

20. Ndipo anthu ambiri anasonkhananso, kotero kuti sanathe iwo konse kudya.

21. Ndipo pamene abale ace anamva, anadza kudzamgwira Iye; pakuti anati adayaruka.

22. Ndipo alembi amene adatsika ku Yerusalemu ananena kuti, Ali naye Beelzibule, ndipo, Ndi mkuru wao wa ziwanda aturutsa ziwanda.

23. Ndipo m'mene adawaitana iwo, ananena nao m'mafanizo, Satana angathe bwanji kuturutsa Satana?

24. Ndipo ufumu ukagawanika pa uwu wokha, sukhoza kukhazikika.

25. Ndipo nyumba ikagawanika pa iyo yokha, siikhoza kukhazikika nyumbayo,

26. Ndipo Satana akadziukira mwini yekha, nagawanika, sakhoza kukhazikika, koma atsirizika.

27. Komatu palibe munthu akhoza kulowa m'nvumba ya mwini mphamvu, ndi kufunkha akatundu ace, koma athange wamanga mwini mphamvuyo; ndipo pamenepo adzafunkha za m'nyumba mwace.

28. Indetu, ndinena ndi inu, Adzakhululukidwa macimo onse a ana a anthu, ndi zamwano ziri zonse adzacita mwano nazo;

29. koma ali yense adzacitira Mzimu Woyera mwano alibe kukhululukidwa nthawi yonse, koma anaparamuladi cimo losatha;

Werengani mutu wathunthu Marko 3