Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Marko 3:10-14 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

10. pakuti adawaciritsa ambiri; kotero kuti onse akukhala nazo zowawa anakanikiza Iye, kuti akamkhudze.

11. Ndipo mizimu yonyansa, m'mene inamuona Iye, inamgwadira, nipfuula, niti, Inu ndinu Mwana wa Mulungu.

12. Ndipo anailimbitsira mau kuti isamuulule Iye.

13. Ndipo anakwera m'phiri, nadziitanira iwo amene anawafuna Iye mwini; ndipo anadza kwa Iye.

14. Ndipo anaika khumi ndi awiri, kuti akhale ndi Iye, ndi kuti akawatume kulalikira,

Werengani mutu wathunthu Marko 3