Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Marko 2:25-28 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

25. Ndipo ananena nao, Simunawerenga konse cimene anacicita Davide, pamene adasowa, namva njala, iye ndi iwo amene anali pamodzi naye?

26. Kuti, analowa m'nyumba ya Mulungu masiku a Abyatara, mkulu wa ansembe, ndipo anadya mikate yoonetsera, yosaloleka kudya ena, koma ansembe okha, ndipo anawapatsanso iwo amene anali naye?

27. Ndipo ananena nao, Sabata linaikidwa cifukwa ca munthu, si munthu cifukwa ca Sabata;

28. motero Mwana wa munthu ali mwini dzuwa la Sabata lomwe.

Werengani mutu wathunthu Marko 2