Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Marko 15:23-30 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

23. Ndipo anampatsa vinyo wosanganiza ndi mure; koma Iye sanamlandira.

24. Ndipo anampacika Iye, nagawana zobvala zace mwa iwo okha, ndi kucita maere pa izo, kuti adziwe yense adzatengaciani.

25. Ndipo panali ora lacitatu, ndipo anampacika Iye.

26. Ndipo lembo la mlandu wace linalembedwa pamwamba, MFUMU YAAYUDA.

27. Ndipo anapacika pamodzi ndi Iye acifwamba awiri; mmodzi ku dzanja lace lamanja ndi wina kulamanzere.[

28. ]

29. Ndipo iwo akupitirirapo anamcitira mwano, napukusa mitu yao, nanena, Ha! iwe wakupasula Kacisi, ndi kummanga masiku atatu,

30. udzipulumutse mwini, nutsike pamtanda.

Werengani mutu wathunthu Marko 15