Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Marko 15:18-31 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

18. ndipo anayamba kumlankhula Iye, kuti, Tikuoneni, Mfumu ya Ayuda!

19. Ndipo anampanda Iye pamutu pace ndi bango, namthira malobvu, nampindira maondo, namlambira.

20. Ndipo atatha kumnyoza anambvula cibakuwaco nambveka Iye zobvala zace. Ndipo anaturuka naye kuti akampacike Iye pamtanda.

21. Ndipo anakangamiza wina wopitirirapo, Simoni wa ku Kurene, alikucokera kuminda, atate wao wa Alesandere ndi Rufu, kuti anyamule mtanda wace.

22. Ndipo anamtenga kunka naye ku malo Golgota, ndiwo, osandulika, Malo-a-bade.

23. Ndipo anampatsa vinyo wosanganiza ndi mure; koma Iye sanamlandira.

24. Ndipo anampacika Iye, nagawana zobvala zace mwa iwo okha, ndi kucita maere pa izo, kuti adziwe yense adzatengaciani.

25. Ndipo panali ora lacitatu, ndipo anampacika Iye.

26. Ndipo lembo la mlandu wace linalembedwa pamwamba, MFUMU YAAYUDA.

27. Ndipo anapacika pamodzi ndi Iye acifwamba awiri; mmodzi ku dzanja lace lamanja ndi wina kulamanzere.[

28. ]

29. Ndipo iwo akupitirirapo anamcitira mwano, napukusa mitu yao, nanena, Ha! iwe wakupasula Kacisi, ndi kummanga masiku atatu,

30. udzipulumutse mwini, nutsike pamtanda.

31. Moteronso ansembe akuru anamtonza mwa iwo okha pamodzi ndi alembi, nanena, Anapulumutsa ena; sakhoza kudzipulumutsa yekha.

Werengani mutu wathunthu Marko 15