Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Marko 15:15-21 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

15. Ndipo Pilato pofuna kuwakhazika mtima anthuwo, anawamasulira Baraba, napereka Yesu, atamkwapula, akampacike pamtanda.

16. Ndipo asilikari anacoka naye nalowa m'bwalo, ndilo Pretorio; nasonkhanitsa gulu lao lonse.

17. Ndipo anambveka Iye cibakuwa, naluka korona waminga, nambveka pa Iye;

18. ndipo anayamba kumlankhula Iye, kuti, Tikuoneni, Mfumu ya Ayuda!

19. Ndipo anampanda Iye pamutu pace ndi bango, namthira malobvu, nampindira maondo, namlambira.

20. Ndipo atatha kumnyoza anambvula cibakuwaco nambveka Iye zobvala zace. Ndipo anaturuka naye kuti akampacike Iye pamtanda.

21. Ndipo anakangamiza wina wopitirirapo, Simoni wa ku Kurene, alikucokera kuminda, atate wao wa Alesandere ndi Rufu, kuti anyamule mtanda wace.

Werengani mutu wathunthu Marko 15