Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Marko 15:13-20 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

13. Ndipo anapfuulanso, Mpacikeni pamtanda.

14. Ndipo Pilato ananena nao, Pakuti Iye anacita coipa cotani? Koma iwo anapfuulitsatu, Mpacikeni Iye.

15. Ndipo Pilato pofuna kuwakhazika mtima anthuwo, anawamasulira Baraba, napereka Yesu, atamkwapula, akampacike pamtanda.

16. Ndipo asilikari anacoka naye nalowa m'bwalo, ndilo Pretorio; nasonkhanitsa gulu lao lonse.

17. Ndipo anambveka Iye cibakuwa, naluka korona waminga, nambveka pa Iye;

18. ndipo anayamba kumlankhula Iye, kuti, Tikuoneni, Mfumu ya Ayuda!

19. Ndipo anampanda Iye pamutu pace ndi bango, namthira malobvu, nampindira maondo, namlambira.

20. Ndipo atatha kumnyoza anambvula cibakuwaco nambveka Iye zobvala zace. Ndipo anaturuka naye kuti akampacike Iye pamtanda.

Werengani mutu wathunthu Marko 15