Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Marko 15:1-8 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ndipo pomwepo mamawa anakhala upo ansembe akuru, ndi akuru a anthu, ndi alembi, ndi akuru a milandu onse, namanga Yesu, namtenga, nampereka kwa Pilato.

2. Ndipo Pilato anamfunsa Iye, Kodi ndiwe Mfumu ya Ayuda? Ndipo anayankha, nanena naye, Mwatero.

3. Ndipo ansembe akuru anamnenera Iye zinthu zambiri.

4. Ndipo Pilato anamfunsanso, nanena, Suyankha kanthu kodi? taona, akunenera Iwe zinthu zambiri zotere.

5. Koma Yesu sanayankhanso kanthu; kotero kuti Pilato anazizwa.

6. Ndipo adafuwamasulira paphwando wandende mmodzi, amene iwo anampempha,

7. Ndipo analipo wina dzina lace Baraba, womangidwa pamodzi ndi opanduka, amene anapha munthu mumphandumo.

8. Ndipo khamu la anthu anabwera nayamba kupempha kuti acite monga adafuwacitira.

Werengani mutu wathunthu Marko 15