Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Marko 15:1-5 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ndipo pomwepo mamawa anakhala upo ansembe akuru, ndi akuru a anthu, ndi alembi, ndi akuru a milandu onse, namanga Yesu, namtenga, nampereka kwa Pilato.

2. Ndipo Pilato anamfunsa Iye, Kodi ndiwe Mfumu ya Ayuda? Ndipo anayankha, nanena naye, Mwatero.

3. Ndipo ansembe akuru anamnenera Iye zinthu zambiri.

4. Ndipo Pilato anamfunsanso, nanena, Suyankha kanthu kodi? taona, akunenera Iwe zinthu zambiri zotere.

5. Koma Yesu sanayankhanso kanthu; kotero kuti Pilato anazizwa.

Werengani mutu wathunthu Marko 15