Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Marko 14:6-15 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

6. Koma Yesu anati, Mlekeni, mumbvutiranji? wandicitira Ine nchito yabwino.

7. Pakuti muli nao aumphawi pamodzi ndi inu masiku onse, ndipo pali ponse pamene mukafuna mukhoza kuwacitira zabwino; koma Ine simuli nane masiku onse.

8. Iye wacita cimene wakhoza; anandidzozeratu thupi langa ku kuikidwa m'manda.

9. Ndipo ndithu ndinena ndi inu, Ponse pamene padzalalikidwa Uthenga Wabwino ku dziko lonse lapansi, icinso cimene anacita mkazi uyu cidzanenedwa, cikhale comkumbukira naco.

10. Ndipo Yudase Isikariote, ndiye mmodzi wa khumi ndi awiriwo, anacoka napita kwa ansembe akuru, kuti akampereke Iye kwa iwo.

11. Ndipo pamene iwo anamva, anasekera, nalonjezana naye kuti adzampatsa ndalama. Ndipo iye anafunafuna pompereka Iye bwino.

12. Ndipo tsiku loyamba la mikate yopanda cotupitsa, pamene amapha Paskha, ophunzira ace ananena naye, Mufuna tinke kuti, tikakonze mkadyereko Paskha?

13. Ndipo anatuma awiri a ophunzira ace, nanena nao, Lowani m'mzinda, ndipo adzakomana nanu munthu wakusenza mtsuko wa madzi; mumtsate iye;

14. ndipo kumene akalowako iye, munene naye mwini nyumba, Mphunzitsi anena, Ciri kuti cipinda ca alendo canga, m'menemo ndikadye Paskha ndi ophunzira anga?

15. Ndipo iye yekha adzakusonyezani cipinda ca pamwamba cacikuru coyalamo ndi cokonzedwa; ndipo m'menemo mutikonzere.

Werengani mutu wathunthu Marko 14