Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Marko 14:49-54 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

49. Masiku onse ndinali nanu m'Kacisi ndirikuphunzitsa, ndipo simunandigwira Ine; koma ici cacitika kuti malembo akwanitsidwe.

50. Ndipo iwo onse anamsiya Iye, nathawa.

51. Ndipo mnyamata wina anamtsata Iye, atapfundira pathupi bafuta yekha; ndipo anamgwira;

52. koma iye anasiya bafutayo, nathawa wamarisece.

53. Ndipo ananka naye Yesu kwa mkulu wa ansembe; ndipo anasonkhana kwa iye ansembe akuru onse ndi akuru a anthu, ndi alembi,

54. Ndipo Petro adamtsata Iye kutali, kufikira kulowa m'bwalo la mkulu wa ansembe; ndipo anali kukhala pansi pamodzi ndi anyamata, ndi kuotha moto.

Werengani mutu wathunthu Marko 14