Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Marko 14:4-7 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

4. Koma anakhalako ena anabvutika mtima mwa iwo okha, ndi kuti, Mafutawo atayidwa cifukwa ninji?

5. Pakuti mafuta amene akadagula marupiya atheka mazana atatu ndi mphambu zace, ndi kupatsa aumphawi. Ndipo anadandaulira mkaziyo.

6. Koma Yesu anati, Mlekeni, mumbvutiranji? wandicitira Ine nchito yabwino.

7. Pakuti muli nao aumphawi pamodzi ndi inu masiku onse, ndipo pali ponse pamene mukafuna mukhoza kuwacitira zabwino; koma Ine simuli nane masiku onse.

Werengani mutu wathunthu Marko 14