Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Marko 14:3-8 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

3. Ndipo pakukhala iye ku Betaniya m'nyumba ya Simoni wakhate, m'mene anaseama kudya, anadzapo mkazi ali nayo nsupa yaalabastero ya mafuta onunkhira bwino a nardo weni weni a mtengowapatali; naswa nsupayo, nawatsanulira pamutu pace.

4. Koma anakhalako ena anabvutika mtima mwa iwo okha, ndi kuti, Mafutawo atayidwa cifukwa ninji?

5. Pakuti mafuta amene akadagula marupiya atheka mazana atatu ndi mphambu zace, ndi kupatsa aumphawi. Ndipo anadandaulira mkaziyo.

6. Koma Yesu anati, Mlekeni, mumbvutiranji? wandicitira Ine nchito yabwino.

7. Pakuti muli nao aumphawi pamodzi ndi inu masiku onse, ndipo pali ponse pamene mukafuna mukhoza kuwacitira zabwino; koma Ine simuli nane masiku onse.

8. Iye wacita cimene wakhoza; anandidzozeratu thupi langa ku kuikidwa m'manda.

Werengani mutu wathunthu Marko 14