Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Marko 14:25-41 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

25. Ndithu ndinena nanu, Sindidzamwanso cipatso ca mpesa, kufikira tsiku lijalo, limene ndidzamwa ico catsopano mu Ufumu wa Mulungu.

26. Ndipo atayimba nyimbo, anaturuka, namuka ku phiri la Azitona.

27. Ndipo Yesu ananena nao, Mudzakhumudwa nonsenu; pakuti kwalembedwa,Ndidzakantha mbusa, ndi nkhosa zidzamwazika.

28. Komatu nditadzauka ndidzatsogolera inu ku Galileya.

29. Koma Petro ananena naye, Angakhale adzakhumudwa onse, komatu ine iai.

30. Ndipo Yesu ananena naye, Ndithu ndinena ndi iwe, kuti lero, usiku uno, tambala asanalire kawiri, udzandikana Ine katatu.

31. Koma iye analimbitsa mau cilimbitsire, kuti, Ngakhale ndidzafa nanu, sindidzakana Inu. Ndipo onsewo anatero.

32. Ndipo iwo anadza ku malo dzina lace Getsemane; ndipo ananena kwa ophunzira ace, Bakhalani pano, kufikira ndikapemphera.

33. Ndipo anatenga pamodzi ndi Iye Petro, ndi Yakobo, ndi Yohane, nayamba kudabwa kwambiri, ndi kusauka mtima ndithu.

34. Ndipo ananena nao, Moyo wanga uli wa cisoni cambiri, kufikira imfa. Bakhalani pano, nimudikire.

35. Ndipo Iye anapita m'tsogolo pang'ono, nagwa pansi, napemphera kuti ngati nkutheka nthawi imene impitirire.

36. Ndipo ananena, Abba, Atate, zinthu zonse zitheka ndi Inu; mundicotsere cikho ici; komatu si cimene ndifuna Ine, koma cimene mufuna Inu.

37. Ndipo anadza nawapeza iwo ali m'tulo, nanena ndi Petro, Simoni, ugona kodi? unalibe mphamvu yakudikira ora limodzi kodi?

38. Dikirani, pempherani, kuti mungalowe m'kuyesedwa; mzimutu uli wakufuna, koma thupi liri lolefuka.

39. Ndipo anacokanso, napemphera, nanena mau omwewo.

40. Ndipo anadzanso nawapeza ali m'tulo, pakuti maso ao analemeradi; ndipo sanadziwa comyankha Iye.

41. Ndipo anadza kacitatu, nanena nao, Gonani tsopano, nimupumule; cakwanira; yafika nthawi; onani Mwana wa munthu aperekedwa m'manja a anthu ocimwa.

Werengani mutu wathunthu Marko 14