Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Marko 14:1-4 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ndipo popita masiku awiri kuli phwando la Paskha ndi mikate yopanda cotupitsa; ndipo ansembe akuru ndi alembi anafunafuna momcitira ciwembu, ndi kumupha:

2. pakuti anati, Paphwando ai, kuti pangakhale phokoso la anthu.

3. Ndipo pakukhala iye ku Betaniya m'nyumba ya Simoni wakhate, m'mene anaseama kudya, anadzapo mkazi ali nayo nsupa yaalabastero ya mafuta onunkhira bwino a nardo weni weni a mtengowapatali; naswa nsupayo, nawatsanulira pamutu pace.

4. Koma anakhalako ena anabvutika mtima mwa iwo okha, ndi kuti, Mafutawo atayidwa cifukwa ninji?

Werengani mutu wathunthu Marko 14