Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Marko 13:34-37 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

34. Monga ngati munthu wa paulendo, adacoka kunyumba kwace, nawapatsa akapolo ace ulamuliro, kwa munthu ali yense nchito yace, nalamulira wapakhomo adikire.

35. Cifukwa cace dikirani; pakuti simudziwa inu nthawi yace yakubwera mwini nyumba, kapena madzulo, kapena pakati pausiku, kapena pakulira tambala, kapena mamawa;

36. kuti angabwere balamantha nakakupezani muli m'tulo.

37. Ndipo cimene ndinena ndi inu ndinena kwa onse, Dikirani.

Werengani mutu wathunthu Marko 13