Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Marko 13:26-31 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

26. Ndipo pamenepo adzaona Mwana wa munthu alinkudza m'mitambo ndi mphamvu yaikuru, ndi ulemerero.

27. Ndipo pamenepo adzatuma angelo, nadzasonkhanitsa osankhidwa ace ocokera ku mphepo zinai, kuyambira ku malekezero ace a dziko lapansi, ndi kufikira ku malekezero a thambo.

28. Ndipo phunzirani ndi mkuyu fanizo lace; pamene pafika kuti nthambi yace ikhala yanthete, ndipo anaphuka masamba ace, muzindikira kuti layandikira dzinja;

29. comweco inunso, pamene muona zinthu izi zirikucitika, zindikirani kuti ali pafupi pakhomo.

30. Indetu ndinena ndi inu, Mbadwo uno sudzapita kufikira zinthu izi zonse zitacitika.

31. Thambo ndi dziko lapansi zidzapita; koma mau anga sadzapita.

Werengani mutu wathunthu Marko 13