Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Marko 13:22-28 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

22. pakuti adzauka Akristu onyenga ndi aneneri onyenga, ndipo adzacita zizindikilo ndi zozizwitsa, kuti akasoceretse, ngati nkutheka, osankhidwa omwe.

23. Koma yanganirani; onani ndakuuziranitu zinthu zonse, zisanafike.

24. Koma m'masikuwo, citatha cisautso cimeneco, dzuwa lidzadetsedwa, ndi mwezi sudzapatsa kuunika kwace,

25. ndi nyenyezi zidzagwa kucokera m'mwamba ndi mphamvu ziri m'mwamba zidzagwedezeka.

26. Ndipo pamenepo adzaona Mwana wa munthu alinkudza m'mitambo ndi mphamvu yaikuru, ndi ulemerero.

27. Ndipo pamenepo adzatuma angelo, nadzasonkhanitsa osankhidwa ace ocokera ku mphepo zinai, kuyambira ku malekezero ace a dziko lapansi, ndi kufikira ku malekezero a thambo.

28. Ndipo phunzirani ndi mkuyu fanizo lace; pamene pafika kuti nthambi yace ikhala yanthete, ndipo anaphuka masamba ace, muzindikira kuti layandikira dzinja;

Werengani mutu wathunthu Marko 13