Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Marko 12:34-39 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

34. Ndipo palmona kuti anayankha ndi nzeru, Yesu anati kwa iye, Suli kutali ndi Ufumu wa Mulungu. Ndipo palibe munthu analimbanso mtima kwnfunsa Iye kanthu.

35. Ndipo Yesu pamene anaphunzitsa m'Kacisi, anayankha, nanena, Bwanji alembi anena kuti Kristu ndiye mwana wa Davide?

36. Davide mwini yekha anati mwa Mzimu Woyera, Ambuye anati kwa Ambuye wanga, Khala ku dzanja langa lamanja, kufikira ndiwaika adani ako popondapo mapazi ako.

37. Davide mwini yekha amchula Iye Ambuye; ndipo ali mwana wace bwanji? Ndipo anthu a makamuwo anakondwa kumva Iye.

38. Ndipo m'ciphunzitso cace ananena, Yang'anirani mupewe alembi, akufuna kuyendayenda obvala miinjiro, ndi kulankhulidwa pamisika,

39. ndi kukhala nayo mipando yaulemu m'sunagoge, ndi malo aulemu pamapwando:

Werengani mutu wathunthu Marko 12