Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Marko 12:20-26 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

20. Analipo abale asanu ndi awiri; woyamba anakwatira mkazi, nafa, wosasiya mbeu;

21. ndipo waciwiri anamkwatira, nafa, wosasiya mbeu; ndipo wacitatunso anatero momwemo;

22. ndipo asanu ndi awiriwo analibe kusiya mbeu. Potsiriza pace pa onse mkazinso anafa.

23. Pakuuka adzakhala mkazi wa yani wa iwowa? Pakuti asanu ndi awiriwo adamuyesa mkazi wao.

24. Yesu ananena nao, Simusocera nanga mwa ici, popeza mulibe kudziwa malembo, kapena mphamvu yace ya Mulungu?

25. Pakuti pamene adzauka kwa akufa, sakwatira, kapena sakwatiwa; koma akhala ngati angelo a Kumwamba. Koma za akufa, kuti akauldtsidwa;

26. simunawerenga m'kalata wa Mose kodi, za Citsambaco, kuti Mulungu anati kwa iye, nanena, Ine Ndine Mulungu wa Abrahamu, ndi Mulungu wa Isake, ndi Mulungu wa Yakobo?

Werengani mutu wathunthu Marko 12