Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Marko 12:19-22 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

19. Mphunzitsi, Mose anatilembera, kuti, Akafa mbale wace wa munthu, nasiya mkazi, wosasiyapo mwana, mbale wace atenge mkazi wace, namuuldtsire mbale waceyo mbeu.

20. Analipo abale asanu ndi awiri; woyamba anakwatira mkazi, nafa, wosasiya mbeu;

21. ndipo waciwiri anamkwatira, nafa, wosasiya mbeu; ndipo wacitatunso anatero momwemo;

22. ndipo asanu ndi awiriwo analibe kusiya mbeu. Potsiriza pace pa onse mkazinso anafa.

Werengani mutu wathunthu Marko 12