Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Marko 12:18-25 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

18. Ndipo anadza kwa Iye Asaduki, amene amanena kuti palibe kuuka kwa akufa; ndipo anamfunsa Iye, nanena,

19. Mphunzitsi, Mose anatilembera, kuti, Akafa mbale wace wa munthu, nasiya mkazi, wosasiyapo mwana, mbale wace atenge mkazi wace, namuuldtsire mbale waceyo mbeu.

20. Analipo abale asanu ndi awiri; woyamba anakwatira mkazi, nafa, wosasiya mbeu;

21. ndipo waciwiri anamkwatira, nafa, wosasiya mbeu; ndipo wacitatunso anatero momwemo;

22. ndipo asanu ndi awiriwo analibe kusiya mbeu. Potsiriza pace pa onse mkazinso anafa.

23. Pakuuka adzakhala mkazi wa yani wa iwowa? Pakuti asanu ndi awiriwo adamuyesa mkazi wao.

24. Yesu ananena nao, Simusocera nanga mwa ici, popeza mulibe kudziwa malembo, kapena mphamvu yace ya Mulungu?

25. Pakuti pamene adzauka kwa akufa, sakwatira, kapena sakwatiwa; koma akhala ngati angelo a Kumwamba. Koma za akufa, kuti akauldtsidwa;

Werengani mutu wathunthu Marko 12