Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Marko 11:24-32 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

24. Cifukwa cace ndinena ndi inu, Zinthu ziri zonse mukazipemphera ndi kuzipempha, khulupirirani kuti mwazilandira, ndipo mudzakhala nazo.

25. Ndipo pamene muimirira ndi kupemphera, kholulukirani, ngati munthu wakulakwirani kanthu; kuti Atate wanunso ali Kumwamba akhulolukire inu zolakwa zanu.

27. Ndipo iwo anadzanso ku Yerusalemu; ndipo m'mene Iye anali kuyenda m'Kacisi, anafika kwa Iye ansembe akuru, ndi alembi ndi akuru;

28. nanena naye, Izi muzicita ndi ulamuliro wotani? Kapena anakupatsani ndani ulamuliro uwu wakucita izi?

29. Ndipo Yesu anati kwa iwo, Ndikufunsani mau amodzi, mundiyankhe Ine, ndipo ndidzakuuzani ulamuliro umene ndicita nao zinthu zimenezi.

30. Ubatizo wa Yohane ucokera Kumwamba kodi, kapena kwa anthu? Mundiyankhe.

31. Ndipo anatsutsana mwa iwo okha, nanena, Tikati, Kumwamba; adzanena iye, Ndipo simunakhulupirira iye bwanji?

32. Koma tikati, Kwa anthu —anaopa anthuwo; pakuti onse anamuyesa Yohane mneneri ndithu.

Werengani mutu wathunthu Marko 11