Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Marko 11:2-6 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

2. nanena nao, Mukani, lowani m'mudzi wapandunji ndi inu; ndipo pomwepo pakulowamo mudzapeza mwana wa buru womangidwa, amene palibe munthu anakhalapo kale lonse; mmasuleni, ndipo mubwere naye.

3. Ndipo munthu akati kwa inu, Mutero bwanji? Katini, Ambuye amfuna iye; ndipo pomwepo adzamtumiza kuno.

4. Ndipo anacoka, napeza mwana wa buru womangidwa pakhomo, pabwalo m'khwalala, nammasula iye.

5. Ndipo ena akuima kumeneko ananena nao, Mucita ciani ndi kumasula mwana wa buru?

6. Ndipo anati kwa iwo monga momwe ananena Yesu: ndipo anawalola iwo apite naye.

Werengani mutu wathunthu Marko 11