Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Marko 10:6-12 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

6. Koma kuyambira pa ciyambi ca malengedwe anawapanga mwamuna ndi mkazi.

7. Cifukwa cace mwamuna adzasiya atate wace ndi amai wace, ndipo adzaphatikizana ndi mkazi wace;

8. ndipo awiriwa adzakhala thupi limodzi: kotero kuti salinso awiri, koma thupi limodzi.

9. Cifukwa cace cimene Mulungu anacimanga pamodzi, asacilekanitse munthu.

10. Ndipo m'nyumba ophunzira anamfunsanso za cinthu ici.

11. Ndipo Iye ananena nao, Munthu ali yense akacotsa mkazi wace, nakakwatira wina, acita cigololo kulakwira mkaziyo;

12. ndipo ngati mkazi akacotsa mwamuna wace, nakwatiwa ndi wina, acita cigololo iyeyu.

Werengani mutu wathunthu Marko 10