Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Marko 10:21-29 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

21. Ndipo Yesu anamyang'ana, namkonda, nati kwa iye, Cinthu cimodzi cikusowa: pita, gulitsa zonse uli nazo, nuzipereke kwa anthu aumphawi, ndipo cuma udzakhala naco m'mwamba; ndipo ukadze kuno, unditsate Ine.

22. Koma nkhope yace inagwa pa mau awa, ndipo anacoka iye wacisoni; pakuti anali mwini cuma cambiri.

23. Ndipo Yesu anaunguzaunguza, nanena ndi ophunzira ace, Okhala naco cuma adzalowa mu Ufumu wa Mulungu ndi kubvuta nanga!

24. Ndipo ophunzirawo anazizwa ndithu ndi mau ace. Koma Yesu anayankhanso nanena nao, Ananu, nkobvuta ndithu kwa iwo akutama cuma kulowa mu Ufumu wa Mulungu!

25. Nkwa pafupi kuti ngamila ipyole diso la singano koposa kuti mwini cuma alowe mu Ufumu wa Mulungu.

26. Ndipo anadabwa, nanena kwa Iye, Ndipo angathe kupulumuka ndani?

27. Yesu anawayang'ana iwo nati, Sikutheka ndi anthu, koma kutheka ndi Mulungu; pakuti zinthu zonse zitheka ndi Mulungu.

28. Petro anayamba kunena naye, Onani, ife tinasiya zonse, ndipo tinakutsatani Inu.

29. Yesu anati, Ndinena ndi inu ndithu, Palibe munthu anasiya nyumba, kapena abale, kapena alongo, kapena amai, kapena atate, kapena ana, kapena minda, cifukwa ca Ine, ndi cifukwa ca Uthenga Wabwinowo,

Werengani mutu wathunthu Marko 10