Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Marko 10:19-22 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

19. Udziwa malamulo: Usaphe, Usacite cigololo, Usabe, Usacite umboni wakunama, Usanyenge, Lemekeza atate wako ndi amako.

20. Ndipo iye anati kwa Iye, Mphunzitsi, zonsezi ndinazisunga kuyambira ndiri mwana.

21. Ndipo Yesu anamyang'ana, namkonda, nati kwa iye, Cinthu cimodzi cikusowa: pita, gulitsa zonse uli nazo, nuzipereke kwa anthu aumphawi, ndipo cuma udzakhala naco m'mwamba; ndipo ukadze kuno, unditsate Ine.

22. Koma nkhope yace inagwa pa mau awa, ndipo anacoka iye wacisoni; pakuti anali mwini cuma cambiri.

Werengani mutu wathunthu Marko 10