Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Marko 10:15-17 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

15. Ndithu ndinena ndi inu, Munthu ali yense wosalandira Ufumu wa Mulungu ngati kamwana, sadzalowamo konse.

16. Ndipo Iye anatiyangata, natidalitsa, ndi kuika manja ace pa ito.

17. Ndipo pamene Iye anaturuka kutsata njira, anamthamangira munthu, namgwadira Iye, namfunsa, Mphunzitsi wabwino, ndidzacita ciani kuti ndilandire moyo wosatha?

Werengani mutu wathunthu Marko 10