Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Marko 10:14-21 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

14. Koma pamene Yesu anaona anakwiya, ndipo anati kwa iwo, Lolani tiana tidze kwa Ine; musatiletse: pakuti Ufumu wa Mulungu uli wa totere.

15. Ndithu ndinena ndi inu, Munthu ali yense wosalandira Ufumu wa Mulungu ngati kamwana, sadzalowamo konse.

16. Ndipo Iye anatiyangata, natidalitsa, ndi kuika manja ace pa ito.

17. Ndipo pamene Iye anaturuka kutsata njira, anamthamangira munthu, namgwadira Iye, namfunsa, Mphunzitsi wabwino, ndidzacita ciani kuti ndilandire moyo wosatha?

18. Ndipo Yesu anati kwa iye, Undicha Ine wabwino bwanji? palibe wabwino koma mmodzi, ndiye Mulungu.

19. Udziwa malamulo: Usaphe, Usacite cigololo, Usabe, Usacite umboni wakunama, Usanyenge, Lemekeza atate wako ndi amako.

20. Ndipo iye anati kwa Iye, Mphunzitsi, zonsezi ndinazisunga kuyambira ndiri mwana.

21. Ndipo Yesu anamyang'ana, namkonda, nati kwa iye, Cinthu cimodzi cikusowa: pita, gulitsa zonse uli nazo, nuzipereke kwa anthu aumphawi, ndipo cuma udzakhala naco m'mwamba; ndipo ukadze kuno, unditsate Ine.

Werengani mutu wathunthu Marko 10