Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Marko 10:1-11 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ndipo ananyamuka Iye kumeneko, nadza ku maiko a ku Yudeya ndi ku tsidya lija la Yordano; ndipo anasonkhananso kwa Iye makamu a anthu; ndipo monga anazolowera, anawaphunzitsanso.

2. Ndipo anadza kwa Iye Afarisi, namfunsa Iye ngati kuloledwa kuti munthu acotse mkazi wace, namuyesa Iye.

3. Ndipo Iye anayankha nati kwa iwo, Kodi Mose anakulamulirani ciani?

4. Ndipo anati, Mose analola kulembera kalata wakulekanira, ndi kumcotsa.

5. Koma Yesu anati kwa iwo, Cifukwa ca kuuma kwa mitima yanu anakulemberani lamulo ili.

6. Koma kuyambira pa ciyambi ca malengedwe anawapanga mwamuna ndi mkazi.

7. Cifukwa cace mwamuna adzasiya atate wace ndi amai wace, ndipo adzaphatikizana ndi mkazi wace;

8. ndipo awiriwa adzakhala thupi limodzi: kotero kuti salinso awiri, koma thupi limodzi.

9. Cifukwa cace cimene Mulungu anacimanga pamodzi, asacilekanitse munthu.

10. Ndipo m'nyumba ophunzira anamfunsanso za cinthu ici.

11. Ndipo Iye ananena nao, Munthu ali yense akacotsa mkazi wace, nakakwatira wina, acita cigololo kulakwira mkaziyo;

Werengani mutu wathunthu Marko 10