Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Marko 1:40-45 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

40. Ndipo anadza kwa Iye wodwala khate, nampempha Iye, namgwadira, ndi kunena ndi Iye, Ngati mufuna mukhoza kundikonza.

41. Ndipo Yesu anagwidwa cifundo, natansa dzanja namkhudza iye, nanena naye, Ndifuna; khala wokonzedwa.

42. Ndipo pomwepo khate linamcoka, ndipo anakonzedwa.

43. Ndipo anamuuzitsa, namturutsa pomwepo,

44. nanena naye, Ona, usati unene kanthu kwa munthu ali yense: koma muka, ukadzionetse kwa wansembe, nupereke pa makonzedwe ako 1 zimene adalamulira Mose, zikhale mboni kwa iwo.

45. Koma 2 iye anaturuka nayamba kulalikira ndithu, ndi kubukitsa mauwo, kotero kuti Yesu sanadziwa kulowansopoyera m'mudzi, koma anakhala padera m'mapululu; ndipo anadza kwa Iye anthu a ku malo onse.

Werengani mutu wathunthu Marko 1