Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Marko 1:27-33 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

27. Ndipo anazizwa onse, kotero kuti anafunsana mwa iwo okha, kuti, Ici nciani? ciphunzitso catsopano! ndi mphamvu alamula ingakhale mizimu yonyansa, ndipo imvera Iye.

28. Ndipo mbiri yace inabuka pompaja ku dziko lonse la Galileya lozungulirapo.

29. Ndipo pomwepo, poturuka m'sunagoge, iwo analowa m'nyumba ya Simoni ndi Andreya pamodzi ndi Yakobo ndi Yohane,

30. Ndipo mpongozi wace wa Simoni anali gone wodwala malungo; ndipo pomwepo anamuuza za iye:

31. ndipo anadza namgwira dzanja, namuutsa; ndipo malungo anamleka, ndipo anawatumikira iwo.

32. Ndipo madzulo, litalowa dzuwa, anadza nao kwa Iye onse akudwala, ndi akugwidwa ndi ziwanda.

33. Ndipo mudzi wonse unasonkhana pakhomo.

Werengani mutu wathunthu Marko 1