Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Marko 1:25-38 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

25. Ndipo Yesu anaudzudzula, kuti, Khala uli cete, nuturuke mwa iye.

26. Ndipo mzimu wonyansa, pomng'amba, ndi kupfuula ndi mau akuru, unaturuka mwa iye.

27. Ndipo anazizwa onse, kotero kuti anafunsana mwa iwo okha, kuti, Ici nciani? ciphunzitso catsopano! ndi mphamvu alamula ingakhale mizimu yonyansa, ndipo imvera Iye.

28. Ndipo mbiri yace inabuka pompaja ku dziko lonse la Galileya lozungulirapo.

29. Ndipo pomwepo, poturuka m'sunagoge, iwo analowa m'nyumba ya Simoni ndi Andreya pamodzi ndi Yakobo ndi Yohane,

30. Ndipo mpongozi wace wa Simoni anali gone wodwala malungo; ndipo pomwepo anamuuza za iye:

31. ndipo anadza namgwira dzanja, namuutsa; ndipo malungo anamleka, ndipo anawatumikira iwo.

32. Ndipo madzulo, litalowa dzuwa, anadza nao kwa Iye onse akudwala, ndi akugwidwa ndi ziwanda.

33. Ndipo mudzi wonse unasonkhana pakhomo.

34. Ndipo anaciritsa anthu ambiri akudwala nthenda za mitundu mitundu, naturutsa ziwanda zambiri; ndipo sanalola ziwandazo zilankhule, cifukwa zinamdziwa Iye.

35. Ndipo m'mawa mwace anauka usikusiku, naturuka namuka kucipululu, napemphera kumeneko.

36. Ndipo Simoni ndi anzace anali naye anamtsata,

37. nampeza, nanena naye, Akufunani inu anthu onse.

38. Ndipo ananena nao, Tiyeni kwina, ku midzi iri pafupi apa, kuti ndilalikire komwekonso; pakuti ndadzera nchito imene.

Werengani mutu wathunthu Marko 1