Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Macitidwe 9:26-29 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

26. Koma m'mene anafika ku Yerusalemu, anayesa kudziphatika kwa ophunzira; ndipo anamuopa iye onse, osakhulupirira kuti ali wophunzira.

27. Koma Bamaba anamtenga, napita naye kwa atumwi, nawafotokozera umo adaonera Ambuye m'njira, ndi kuti analankhula naye, ndi kuti m'Damasiko adanena molimbika mtima m'dzina la Yesu.

28. Ndipo anali pamodzi nao, nalowa naturuka ku Yerusalemu,

29. nanena molimbika mtima m'dzina la Ambuye; ndipotu analankhula natsutsana ndi Aheleniste; koma anayesayesa kumupha iye.

Werengani mutu wathunthu Macitidwe 9