22. Koma Saulo anakula makamaka mumphamvu, nadodometsa Ayuda akukhala m'Damasiko, nawatsimikizira kuti ameneyo ndi Kristu.
23. Ndipo atapita masiku ambiri, Ayuda anapangana kuti amuphe iye;
24. koma ciwembu cao cinadziwika ndi Saulo. Ndipo anadikiranso pazipata usana ndi usiku kuti amuphe;
25. koma ophunzira ace anamtenga usiku, nampyoletsa palinga, namtsitsa ndi mtanga,
26. Koma m'mene anafika ku Yerusalemu, anayesa kudziphatika kwa ophunzira; ndipo anamuopa iye onse, osakhulupirira kuti ali wophunzira.