Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Macitidwe 8:5-11 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

5. Ndipo Filipo anatsikira ku mudzi wa ku Samarlya, nawalalikira iwo Kristu.

6. Ndipo makamuwo ndi mtima umodzi anasamalira zonenedwa ndi Filipo, pamene anamva, napenya zizindikilo zimene anazicita.

7. Pakuti ambiri a iwo akukhala nayo mizimu yonyansa inawaturukira, yopfuula ndi mau akuru; ndipo ambiri amanjenje, ndi opunduka, anaciritsidwa.

8. Ndipo panakhala cimwemwe cacikuru m'mudzimo.

9. Koma panali munthu dzina lace Simoni amene adacita matsenga m'mudzimo kale, nadabwitsa anthu a Samariya, ndi kunena kuti iye yekha ndiye munthu wamkuru;

10. ameneyo anamsamalira onsewo, kuyambira wamng'ono kufikira wamkuru, ndi kunena, Uyu ndiye mphamvu ya Mulungu, yonenedwa Yaikuru.

11. Ndipo anamsamalira iye, popeza nthawi yaikuru adawadabwitsa iwo ndi matsenga ace.

Werengani mutu wathunthu Macitidwe 8